< Masalimo 72 >

1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Of Solomon - O God judgments your to [the] king give and righteousness your to [the] son of [the] king.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
He will judge people your with righteousness and poor [people] your with justice.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
They will carry mountains peace to the people and hills in righteousness.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
He will judge - [the] poor [people] of [the] people he will save [the] children of [the] needy so he may crush [the] oppressor.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
People will fear you with [the] sun and before [the] moon generation of generations.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
He will come down like rain on mown grass like copious showers dropping of [the] earth.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
He will flourish in days his [the] righteous and abundance of well-being [will be] until not [the] moon.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
And may he rule from sea to sea and from [the] river to [the] ends of [the] earth.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
Before him they will bow down desert-dwellers and enemies his dust they will lick up.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
[the] kings of Tarshish and [the] islands tribute they will pay [the] kings of Sheba and Seba a gift they will bring near.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
And they may bow down to him all kings all nations they will serve him.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
For he will deliver [the] needy [who] cries for help and [the] poor and not a helper [belongs] to him.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
He will have compassion on [the] poor and [the] needy and [the] lives of needy [people] he will save.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
From oppression and from violence he will redeem life their and may be precious blood their in view his.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
And may he live and he may give to him some of [the] gold of Sheba and [may] someone pray for him continually all the day may someone bless him.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
May it be an abundance of grain - in the land on [the] top of [the] mountains may it wave like Lebanon fruit its and may people blossom from [the] city like [the] vegetation of the earth.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
May it be name his for ever before [the] sun (may it increase *Q(K)*) name his and may they bless themselves by him all nations may they call blessed him.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
[be] blessed - Yahweh God [the] God of Israel [who] does wonders to only him.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
And [be] blessed - [the] name of glory his for ever and may it be filled glory his all the earth amen - and amen.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
They are finished [the] prayers of David [the] son of Jesse.

< Masalimo 72 >