< Masalimo 72 >

1 Salimo la Solomoni. Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo, Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
Of Solomon. Endow the king with Your justice, O God, and the son of the king with Your righteousness.
2 Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo, anthu anu ozunzika mosakondera.
May he judge Your people with righteousness and Your afflicted with justice.
3 Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu, timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
May the mountains bring peace to the people, and the hills bring righteousness.
4 Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu ndi kupulumutsa ana a anthu osowa; adzaphwanya ozunza anzawo.
May he vindicate the afflicted among the people; may he save the children of the needy and crush the oppressor.
5 Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse, nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
May they fear him as long as the sun shines, as long as the moon remains, through all generations.
6 Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
May he be like rain that falls on freshly cut grass, like spring showers that water the earth.
7 Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika; chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
May the righteous flourish in his days and prosperity abound, until the moon is no more.
8 Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
May he rule from sea to sea, and from the Euphrates to the ends of the earth.
9 Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
May the nomads bow before him, and his enemies lick the dust.
10 Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali adzabweretsa mitulo kwa iye, mafumu a ku Seba ndi Seba adzapereka mphatso kwa iyeyo.
May the kings of Tarshish and distant shores bring tribute; may the kings of Sheba and Seba offer gifts.
11 Mafumu onse adzamuweramira ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
May all kings bow down to him and all nations serve him.
12 Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira, wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
For he will deliver the needy who cry out and the afflicted who have no helper.
13 Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
He will take pity on the poor and needy and save the lives of the oppressed.
14 Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
He will redeem them from oppression and violence, for their blood is precious in his sight.
15 Iye akhale ndi moyo wautali; golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye. Anthu amupempherere nthawi zonse ndi kumudalitsa tsiku lonse.
Long may he live! May gold from Sheba be given him. May people ever pray for him; may they bless him all day long.
16 Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse; pamwamba pa mapiri pakhale tirigu. Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni; zichuluke ngati udzu wakuthengo
May there be an abundance of grain in the land; may it sway atop the hills. May its fruit trees flourish like the forests of Lebanon, and its people like the grass of the field.
17 Dzina lake likhazikike kwamuyaya, lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa. Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
May his name endure forever; may his name continue as long as the sun shines. In him may all nations be blessed; may they call him blessed.
18 Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
Blessed be the LORD God, the God of Israel, who alone does marvelous deeds.
19 Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake. Ameni ndi Ameni.
And blessed be His glorious name forever; may all the earth be filled with His glory. Amen and amen.
20 Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
Thus conclude the prayers of David son of Jesse.

< Masalimo 72 >