< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Herre, jag förtröstar uppå dig, låt mig aldrig på skam komma.
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Fräls mig genom dina rättfärdighet, och hjelp mig ut; böj din öron till mig, och hjelp mig.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Var mig en stark tröst, dit jag alltid fly må, du som lofvat hafver att hjelpa mig; ty du äst min klippa och min borg.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Min Gud, hjelp mig utu dens ogudaktigas hand, utu dens orättfärdigas och tyrannens hand.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Ty du äst min tillflykt, Herre, Herre; mitt hopp allt ifrå minom ungdom.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
Uppå dig hafver jag förlåtit mig, allt ifrå moderlifvet; du hafver dragit mig utu mine moders lif; min berömmelse är alltid af dig.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
Jag är för mångom ett vidunder; men du äst min starka tröst.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
Låt min mun full vara af ditt lof och pris dagliga dags.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Förkasta mig icke uti min ålderdom; öfvergif mig icke, när jag svag varder.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
Ty mine fiender tala emot mig, och de som efter mina själ vakta, de rådslå tillhopa;
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Och säga: Gud hafver öfvergifvit honom; jager efter, och griper honom; ty der är ingen hjelpare.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
Gud, var icke långt borto ifrå mig; min Gud, skynda dig till att hjelpa mig.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Skämme sig och förgås, de som emot mine själ äro; varde med skam och hån öfvertäckte, de som mitt värsta söka.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
Men jag vill alltid bida, och vill alltid föröka ditt lof.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Min mun skall förkunna dina rättfärdighet, dagliga dags dina salighet, den jag icke alla räkna kan.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Jag går i Herrans, Herrans kraft; jag prisar dina rättfärdighet, ja, din allena.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
Gud, du hafver lärt mig af min ungdom; derföre förkunnar jag ännu din under.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Ock förlåt mig icke, Gud, i ålderdomen, när jag grå varder; tilldess jag förkunnar din arm barnabarnom, och dina magt allom dem som komma skola.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Gud, din rättfärdighet är hög, du som stor ting gör. Gud, ho är dig lik?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Ty du låter mig förfara mycken och stor ångest, och gör mig åter lefvande; och hemtar mig åter upp utu jordenes djup.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Du gör mig ganska storan, och styrker mig igen.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
Så tackar jag ock dig med psaltarespel, för dina trofasthet, min Gud. Jag lofsjunger dig på harpor, du Helige i Israel.
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
Mine läppar och min själ, som du förlöst hafver, äro glade, och lofsjunga dig.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
Ock talar min tunga dagliga dags om dina rättfärdighet; ty skämma måga sig, och på skam komma, de som mitt värsta söka.

< Masalimo 71 >