< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Ын Тине, Доамне, ымь каут скэпаря: сэ ну рэмын де рушине ничодатэ!
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Скапэ-мэ ын дрептатя Та ши избэвеште-мэ! Плякэ-Ць урекя спре мине ши ажутэ-мь.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Фий о стынкэ де адэпост пентру мине, унде сэ пот фуӂи тотдяуна! Ту ай хотэрыт сэ мэ скапь, кэч Ту ешть стынка ши четэцуя мя.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Избэвеште-мэ, Думнезеуле, дин мына челуй рэу, дин мына омулуй нелеӂюит ши асупритор!
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Кэч Ту ешть нэдеждя мя, Доамне Думнезеуле! Ын Тине мэ ынкред дин тинереця мя.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
Пе Тине мэ сприжин дин пынтечеле мамей меле. Ту ешть Бинефэкэторул меу ынкэ дин пынтечеле мамей; пе Тине Те лауд фэрэ-нчетаре.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
Пентру мулць, ам ажунс ка о минуне, дар Ту ешть скэпаря мя чя таре.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
Сэ ми се умпле гура де лауделе Тале ши-н фиекаре зи сэ Те слэвяскэ!
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Ну мэ лепэда ла время бэтрынеций; кынд ми се дук путериле, ну мэ пэрэси!
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
Кэч врэжмаший мей ворбеск де мине ши чей че-мь пындеск вяца се сфэтуеск ынтре ей
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
зикынд: „Л-а пэрэсит Думнезеу; урмэрици-л, пунець мына пе ел, кэч ну-й нимень каре сэ-л скапе!”
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
Думнезеуле, ну Те депэрта де мине! Думнезеуле, вино деграбэ ын ажуторул меу!
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Сэ рэмынэ де рушине ши нимичиць чей че вор сэ-мь я вяца! Сэ фие акопериць де рушине ши де окарэ чей че-мь каутэ перзаря!
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
Ши еу вой нэдэждуи пуруря, Те вой лэуда тот май мулт.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Гура мя ва вести зи де зи дрептатя ши мынтуиря Та, кэч ну ле куноск марӂиниле.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Вой спуне лукрэриле Тале челе путерниче, Доамне Думнезеуле! Вой помени дрептатя Та ши нумай пе а Та!
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
Думнезеуле, Ту м-ай ынвэцат дин тинереце, ши пынэ акум еу вестеск минуниле Тале.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Ну мэ пэрэси, Думнезеуле, кяр ла бэтрынеця кэрунтэ, ка сэ вестеск тэрия Та нямулуй де акум ши путеря Та нямулуй де оамень каре ва вени!
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Дрептатя Та, Думнезеуле, ажунӂе пынэ ла чер. Ту ай сэвыршит лукрурь марь: Думнезеуле, чине есте ка Тине?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Не-ай фэкут сэ тречем прин мулте неказурь ши ненорочирь, дар не вей да ярэшь вяца, не вей скоате ярэшь дин адынкуриле пэмынтулуй.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Ыналцэ-мь мэримя мя, ынтоарче-Те ши мынгые-мэ дин ноу!
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
Ши Те вой лэуда ын сунет де алэутэ, Ыць вой кынта крединчошия. Думнезеуле, Те вой лэуда ку харпа, Сфынтул луй Исраел!
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
Кынд Те вой лэуда, вой фи ку букурия пе бузе, ку букурия ын суфлетул пе каре ми л-ай избэвит;
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
ши лимба мя ва вести зи де зи дрептатя Та, кэч чей че-мь каутэ перзаря сунт рушинаць ши роший де рушине.

< Masalimo 71 >