< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Éternel! je cherche en toi mon refuge: Que jamais je ne sois confondu!
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Dans ta justice, sauve-moi et délivre-moi! Incline vers moi ton oreille, et secours-moi!
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Sois pour moi un rocher qui me serve d’asile, Où je puisse toujours me retirer! Tu as résolu de me sauver, Car tu es mon rocher et ma forteresse.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Mon Dieu, délivre-moi de la main du méchant, De la main de l’homme inique et violent!
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Car tu es mon espérance, Seigneur Éternel! En toi je me confie dès ma jeunesse.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
Dès le ventre de ma mère je m’appuie sur toi; C’est toi qui m’as fait sortir du sein maternel; Tu es sans cesse l’objet de mes louanges.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
Je suis pour plusieurs comme un prodige, Et toi, tu es mon puissant refuge.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
Que ma bouche soit remplie de tes louanges, Que chaque jour elle te glorifie!
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Ne me rejette pas au temps de la vieillesse; Quand mes forces s’en vont, ne m’abandonne pas!
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
Car mes ennemis parlent de moi, Et ceux qui guettent ma vie se consultent entre eux,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Disant: Dieu l’abandonne; Poursuivez, saisissez-le; il n’y a personne pour le délivrer.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
O Dieu, ne t’éloigne pas de moi! Mon Dieu, viens en hâte à mon secours!
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Qu’ils soient confus, anéantis, ceux qui en veulent à ma vie! Qu’ils soient couverts de honte et d’opprobre, ceux qui cherchent ma perte!
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
Et moi, j’espérerai toujours, Je te louerai de plus en plus.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Ma bouche publiera ta justice, ton salut, chaque jour, Car j’ignore quelles en sont les bornes.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Je dirai tes œuvres puissantes, Seigneur Éternel! Je rappellerai ta justice, la tienne seule.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
O Dieu! Tu m’as instruit dès ma jeunesse, Et jusqu’à présent j’annonce tes merveilles.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Ne m’abandonne pas, ô Dieu! Même dans la blanche vieillesse, Afin que j’annonce ta force à la génération présente, Ta puissance à la génération future!
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Ta justice, ô Dieu! Atteint jusqu’au ciel; Tu as accompli de grandes choses: ô Dieu! Qui est semblable à toi?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Tu nous as fait éprouver bien des détresses et des malheurs; Mais tu nous redonneras la vie, Tu nous feras remonter des abîmes de la terre.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Relève ma grandeur, Console-moi de nouveau!
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
Et je te louerai au son du luth, je chanterai ta fidélité, mon Dieu, Je te célébrerai avec la harpe, Saint d’Israël!
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
En te célébrant, j’aurai la joie sur les lèvres, La joie dans mon âme que tu as délivrée;
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
Ma langue chaque jour publiera ta justice, Car ceux qui cherchent ma perte sont honteux et confus.

< Masalimo 71 >