< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
En toi, Éternel! j’ai mis ma confiance: que je ne sois jamais confus!
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Dans ta justice, délivre-moi et fais que j’échappe; incline ton oreille vers moi et sauve-moi.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Sois pour moi un rocher d’habitation, afin que j’y entre continuellement; tu as donné commandement de me sauver, car tu es mon rocher et mon lieu fort.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Mon Dieu! fais-moi échapper de la main du méchant, de la main de l’injuste et de l’oppresseur.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Car toi tu es mon attente, Seigneur Éternel! ma confiance dès ma jeunesse.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
Je me suis appuyé sur toi dès le ventre; c’est toi qui m’as tiré hors des entrailles de ma mère: tu es le sujet continuel de ma louange.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
Je suis pour plusieurs comme un prodige; mais toi, tu es mon fort refuge.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
Ma bouche est pleine de ta louange [et] de ta magnificence, tout le jour.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Ne me rejette pas au temps de [ma] vieillesse; ne m’abandonne pas quand ma force est consumée.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
Car mes ennemis parlent contre moi, et ceux qui guettent mon âme consultent ensemble,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Disant: Dieu l’a abandonné; poursuivez-le et saisissez-le, car il n’y a personne qui le délivre.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
Ô Dieu! ne te tiens pas loin de moi; mon Dieu, hâte-toi de me secourir!
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Qu’ils soient honteux, qu’ils soient consumés, ceux qui sont ennemis de mon âme; qu’ils soient couverts d’opprobre et de confusion, ceux qui cherchent mon malheur.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
Mais moi, j’attendrai continuellement, et je redirai sans cesse toutes tes louanges.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Ma bouche racontera tout le jour ta justice [et] ton salut, car je n’en connais pas l’énumération.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
J’irai dans la puissance du Seigneur Éternel; je ferai mention de ta justice, de la tienne seule.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
Ô Dieu! tu m’as enseigné dès ma jeunesse; et jusqu’ici j’ai annoncé tes merveilles.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Et aussi, jusqu’à la vieillesse et aux cheveux blancs, ô Dieu! ne m’abandonne pas, jusqu’à ce que j’annonce ton bras à [cette] génération, ta puissance à tous ceux qui viendront.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Et ta justice, ô Dieu! est haut élevée. Toi qui as fait de grandes choses, ô Dieu! qui est comme toi?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Toi qui nous as fait voir de nombreuses et amères détresses, tu nous redonneras la vie, et tu nous feras remonter hors des profondeurs de la terre.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Tu multiplieras ma grandeur, et tu te tourneras, tu me consoleras.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
Aussi, mon Dieu, je te célébrerai avec le luth, [je louerai] ta vérité; je chanterai tes louanges avec la harpe, ô Saint d’Israël!
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
Mes lèvres, et mon âme, que tu as rachetée, exulteront quand je chanterai tes louanges.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
Ma langue aussi redira tout le jour ta justice; car ils seront honteux, car ils seront confondus, ceux qui cherchent mon malheur.

< Masalimo 71 >