< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Lord, Y hopide in thee, be Y not schent with outen ende;
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
in thi riytwisnesse delyuere thou me, and rauysche me out. Bowe doun thin eere to me; and make me saaf.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Be thou to me in to God a defendere; and in to a strengthid place, that thou make me saaf. For thou art my stidefastnesse; and my refuit.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
My God, delyuere thou me fro the hoond of the synner; and fro the hoond of a man doynge ayens the lawe, and of the wickid man.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
For thou, Lord, art my pacience; Lord, thou art myn hope fro my yongthe.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
In thee Y am confermyd fro the wombe; thou art my defendere fro the wombe of my modir.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
My syngyng is euere in thee; Y am maad as a greet wonder to many men; and thou art a strong helpere.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
My mouth be fillid with heriyng; that Y synge thi glorie, al dai thi greetnesse.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Caste thou not awei me in the tyme of eldnesse; whanne my vertu failith, forsake thou not me.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
For myn enemyes seiden of me; and thei that kepten my lijf maden counsel togidere.
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Seiynge, God hath forsake hym; pursue ye, and take hym; for noon is that schal delyuere.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
God, be thou not maad afer fro me; my God, biholde thou in to myn help.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Men that bacbiten my soule, be schent, and faile thei; and be thei hilid with schenschip and schame, that seken yuels to me.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
But Y schal hope euere; and Y schal adde euere ouer al thi preising.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
Mi mouth schal telle thi riytfulnesse; al dai thin helthe. For Y knewe not lettrure, Y schal entre in to the poweres of the Lord;
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Lord, Y schal bithenke on thi riytfulnesse aloone.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
God, thou hast tauyt me fro my yongthe, and `til to now; Y schal telle out thi merueilis.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
And til in to `the eldnesse and the laste age; God, forsake thou not me. Til Y telle thin arm; to eche generacioun, that schal come. Til Y telle thi myyt,
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
and thi riytfulnesse, God, til in to the hiyeste grete dedis which thou hast do; God, who is lijk thee?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Hou grete tribulaciouns many and yuele hast thou schewid to me; and thou conuertid hast quykenyd me, and hast eft brouyt me ayen fro the depthis of erthe.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Thou hast multiplied thi greet doyng; and thou conuertid hast coumfortid me.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
For whi and Y schal knowleche to thee, thou God, thi treuthe in the instrumentis of salm; Y schal synge in an harpe to thee, that art the hooli of Israel.
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
Mi lippis schulen make fulli ioye, whanne Y schal synge to thee; and my soule, which thou ayen bouytist.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
But and my tunge schal thenke al dai on thi riytfulnesse; whanne thei schulen be schent and aschamed, that seken yuelis to me.

< Masalimo 71 >