< Masalimo 71 >
1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
Yahweh, I have come to you to (get refuge/be protected); never allow me to become ashamed [because of being defeated].
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Because you always do what is right, help me and rescue me; listen to me, and save me!
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Be [like an overhanging] rock [MET] under which I [can be] safe/protected; [be like] a strong fortress in which I am safe [DOU]. You [continually] command (OR, [Continually] command) [your angels] to rescue me.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
God, rescue me from wicked [people], from the power of unjust and evil men.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
Yahweh, my Lord, you are the one whom I confidently expect [to help me]; I have trusted in you since I was young.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
I have depended on you all my life; you have taken care of me [IDM] since the day that I was born, [so] I will always praise you.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
The manner in which I have conducted my life has been an example to many [people], because [they realize that] you have been my strong defender.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
I praise you all day long, and I proclaim that you are glorious/wonderful.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Now, when I have become an old man, do not reject/abandon me; do not abandon me now, when I am not strong any more.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
My enemies say [that they want to kill] me; they plan together [how they can do that].
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
They say [about me], “God has abandoned him; so now we can pursue him and seize him, because there is no one who will rescue him.”
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
God, do not stay far away from me; hurry to help me!
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Cause those who (accuse me/say that I have done things that are wrong) to be defeated and destroyed; cause those who want to harm me to be shamed and disgraced.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
But [as for me], I will continually and confidently expect [you to do great things for me], and I will praise you more and more.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
I will tell people that you do what is right; all day long I will tell people how you have saved me, although what you have done is more than I can fully understand.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
Yahweh, my Lord, I will praise you for your mighty deeds; I will proclaim that only you always act justly.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
God, you have taught me [many/those things] ever since I was young, and I still tell people about your wonderful deeds.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
And now, God, when I am old and my hair is gray, do not abandon me. [Stay with me] while I continue to proclaim to my children and grandchildren [HYP] that you are [very] powerful!
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
God, you do many righteous deeds; [it is as though] they extend up to the sky. You have done great things; there is no one like you [RHQ].
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
You have caused me to have many troubles and to suffer much, [but] you will cause me to become strong again; when I am almost dead [HYP], you will keep me alive.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
You will cause me to be greatly honored and you will encourage/comfort me again.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
I will also praise you [while I play] my harp; I will praise you, my God, for faithfully [doing what you have promised to do]. I will play hymns to praise you, the holy God whom [we] Israelis [worship].
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
I [SYN] will shout joyfully while I play [the harp] for you; with my entire inner being I will sing because you have rescued me.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
All day long I will tell people that you act righteously, because those who wanted to harm me will have been defeated and disgraced.