< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
In You, O LORD, I have taken refuge; let me never be put to shame.
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
In Your justice, rescue and deliver me; incline Your ear and save me.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Be my rock of refuge, where I can always go. Give the command to save me, for You are my rock and my fortress.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Deliver me, O my God, from the hand of the wicked, from the grasp of the unjust and ruthless.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
For You are my hope, O Lord GOD, my confidence from my youth.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
I have leaned on You since birth; You pulled me from my mother’s womb. My praise is always for You.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
I have become a portent to many, but You are my strong refuge.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
My mouth is filled with Your praise and with Your splendor all day long.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Do not discard me in my old age; do not forsake me when my strength fails.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
For my enemies speak against me, and those who lie in wait for my life conspire,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
saying, “God has forsaken him; pursue him and seize him, for there is no one to rescue him.”
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
Be not far from me, O God. Hurry, O my God, to help me.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
May the accusers of my soul be ashamed and consumed; may those who seek my harm be covered with scorn and disgrace.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
But I will always hope and will praise You more and more.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
My mouth will declare Your righteousness and Your salvation all day long, though I cannot know their full measure.
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
I will enter in the strength of the Lord GOD; I will proclaim Your righteousness—Yours alone.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
O God, You have taught me from my youth, and to this day I proclaim Your marvelous deeds.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Even when I am old and gray, do not forsake me, O God, until I proclaim Your power to the next generation, Your might to all who are to come.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Your righteousness reaches to the heavens, O God, You who have done great things. Who, O God, is like You?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Though You have shown me many troubles and misfortunes, You will revive me once again. Even from the depths of the earth You will bring me back up.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
You will increase my honor and comfort me once again.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
So I will praise You with the harp for Your faithfulness, O my God; I will sing praise to You with the lyre, O Holy One of Israel.
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
When I sing praise to You my lips will shout for joy, along with my soul, which You have redeemed.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
My tongue will indeed proclaim Your righteousness all day long, for those who seek my harm are disgraced and confounded.

< Masalimo 71 >