< Masalimo 71 >

1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
上主,我託庇於您,使我永不受羞恥!
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
求您照您的正義解救我,求您側耳聽我,並拯救我。
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
求您作我避難的石壁,獲救的堡壘;因為您是我的磐石,我的堡壘,
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
我的天主,求您由邪惡人的手中將我救出,由兇蠻橫暴者的掌中將我救走。
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
因為,我主上主,您是我的期望,您是我自幼唯一的仰仗。
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
我自從在母胎中,就仰賴您,尚在母懷中,您就是我的託庇;我全心的希望,時時寄托於您。
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
許多人都把我視作妖怪,您卻作了我有力的仰賴。
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
我要滿口讚頌您,我要終日稱揚您。
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
在我年老時,求您不要拋棄我,在我氣力衰弱時,不要遠離我。
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
不然,我的仇敵必要對我說,窺伺我命的人,互相私議說:
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
天主已經捨棄了他,您們追擊他,捕捉他! 因為無人再來救他。
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
天主,求您不要遠離我,我的天主,請快來救我。
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
願那些謀殺我命的人,走頭無路,願那些設法害我的人,蒙受恥辱!
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
我仍不斷地期望您,每日加倍地讚美您。
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
我的口要傳述您的寬仁,終日不斷宣揚您的救恩,因為我不知它們的數額。
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
我要稱揚我天主的偉大奇能,上主,我要傳述您獨有的寬仁。
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
天主,遠自我幼年時,您已教導了我。直至今日,我仍宣示您的微妙。
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
天主,即我髮白年老,求您也不要離棄我,直至我將您的威力宣示給這一代,將您的奇能傳述給下一代。
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
天主,您的仁慈直達天際,天主,您行大事誰可比您?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
您曾使我經歷許多困苦艱難,現今仍然是您使我生活安全,並提拔我脫離了地下的深淵。
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
求您增加我的尊位,求您再來給我安慰。
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
我的天主,我要彈琴,歌頌您的忠誠,以色列的聖者,我要鼓瑟,向您歌頌。
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
當我歌頌您時,我的雙唇要歡騰,我那為您所救的靈魂,也要歡騰。
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
我的舌頭也要終日伸述您的仁慈,因為謀圖傷害我的人蒙受了羞恥。

< Masalimo 71 >