< Masalimo 70 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
En Psalm Davids, till att föresjunga, till åminnelse. Skynda dig, Gud, till att frälsa mig; Herre, till att hjelpa mig.
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
Skämme sig, och komme på skam, de som efter mine själ stå; vände tillrygga, och komme på skam, de mig ondt önska;
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
Att de måtte på skam komma igen, som öfver mig ropa: Så, så.
4 Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
Fröjde, och glädje sig i dig, de som efter dig fråga; och de som dina salighet älska, säga alltid: Gud vare högeliga lofvad.
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.
Men jag är eländig och fattig; Gud, var snar till mig; ty du äst min hjelpare och förlossare; min Herre, fördröj icke.