< Masalimo 70 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
برای سالار مغنیان. مزمور داود به جهت یادگاری خدایا، برای نجات من بشتاب! ای خداوند به اعانت من تعجیل فرما!۱
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
آنانی که قصد جان من دارند، خجل و شرمنده شوند، و آنانی که در بدی من رغبت دارند، روبرگردانیده و رسوا گردند،۲
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
و آنانی که هه هه می‌گویند، به‌سبب خجالت خویش رو برگردانیده شوند.۳
4 Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
و اما جمیع طالبان تو، در تو وجد و شادی کنند، و دوست دارندگان نجات تو دائم گویند: «خدا متعال باد!»۴
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.
و اما من مسکین و فقیر هستم. خدایا برای من تعجیل کن. تو مددکار ونجات‌دهنده من هستی. ای خداوند تاخیر منما.۵

< Masalimo 70 >