< Masalimo 70 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
Alang sa pangulong musikero. Ang salmo ni David; alang sa paghinumdom. Luwasa ako, O Dios! Yahweh, dali dayon ug tabangi ako.
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
Tugoti nga kadtong mosulay sa pagkuha sa akong kinabuhi mapaulawan ug pagatamastamasan; motalikod unta (sila) ug dad-on sa kaulawan, kadtong nagmalipayon sa akong kasakitan.
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
Motalikod unta (sila) tungod sa ilang kaulaw, kadtong mga nagkatawa.
4 Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
Ang tanan nga nagapangita kanimo maglipay unta ug magmaya diha kanimo; kadtong nahigugma sa imong kaluwasan kanunay unta nga magasulti, “Dalayegon ang Dios.”
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.
Apan kabos ako ug timawa; pagdali nganhi kanako, Dios; ikaw ang akong magtatabang ug luwasa ako. Yahweh, ayaw paglangan.