< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
Псалом Давиду, егоже воспет Господеви о словесех Хусиевых, сына Иемениина. Господи Боже мой, на Тя уповах, спаси мя от всех гонящих мя и избави мя:
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
да не когда похитит яко лев душу мою, не сущу избавляющу, ниже спасающу.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Господи Боже мой, аще сотворих сие, аще есть неправда в руку моею,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
аще воздах воздающым ми зла, да отпаду убо от враг моих тощь:
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
да поженет убо враг душу мою, и да постигнет, и поперет в землю живот мой, и славу мою в персть вселит.
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Воскресени, Господи, гневом Твоим, вознесися в концах враг Твоих, и востани, Господи Боже мой, повелением, имже заповедал еси,
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
и сонм людий обыдет Тя: и о том на высоту обратися.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Господь судит людем: суди ми, Господи, по правде моей и по незлобе моей на мя.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Да скончается злоба грешных, и исправиши праведнаго, испытаяй сердца и утробы, Боже, праведно.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Помощь моя от Бога, спасающаго правыя сердцем.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
Бог судитель праведен и крепок, и долготерпелив, и не гнев наводяй на всяк день.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Аще не обратитеся, оружие Свое очистит, лук Свой напряже, и уготова и,
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
и в нем уготова сосуды смертныя, стрелы Своя сгараемым содела.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Се, боле неправдою, зачат болезнь и роди беззаконие:
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
ров изры и ископа и, и падет в яму, юже содела.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Обратится болезнь его на главу его, и на верх его неправда его снидет.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Исповемся Господеви по правде Его и пою имени Господа Вышняго.