< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
Psalmus David, quem cantavit Domino pro verbis Chusi, filii Jemini. Domine Deus meus, in te speravi; salvum me fac ex omnibus persequentibus me, et libera me:
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
nequando rapiat ut leo animam meam, dum non est qui redimat, neque qui salvum faciat.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Domine Deus meus, si feci istud, si est iniquitas in manibus meis,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
si reddidi retribuentibus mihi mala, decidam merito ab inimicis meis inanis.
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
Persequatur inimicus animam meam, et comprehendat; et conculcet in terra vitam meam, et gloriam meam in pulverem deducat.
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Exsurge, Domine, in ira tua, et exaltare in finibus inimicorum meorum: et exsurge, Domine Deus meus, in præcepto quod mandasti,
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
et synagoga populorum circumdabit te: et propter hanc in altum regredere:
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Dominus judicat populos. Judica me, Domine, secundum justitiam meam, et secundum innocentiam meam super me.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Consumetur nequitia peccatorum, et diriges justum, scrutans corda et renes, Deus.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Justum adjutorium meum a Domino, qui salvos facit rectos corde.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
Deus judex justus, fortis, et patiens; numquid irascitur per singulos dies?
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Nisi conversi fueritis, gladium suum vibrabit; arcum suum tetendit, et paravit illum.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
Et in eo paravit vasa mortis, sagittas suas ardentibus effecit.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Ecce parturiit injustitiam; concepit dolorem, et peperit iniquitatem.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
Lacum aperuit, et effodit eum; et incidit in foveam quam fecit.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Convertetur dolor ejus in caput ejus, et in verticem ipsius iniquitas ejus descendet.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Confitebor Domino secundum justitiam ejus, et psallam nomini Domini altissimi.