< Masalimo 7 >

1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
[Psalm lal David, su el Onkakin nu sin LEUM GOD, ke sripal Cush, sie Mwet Benjamin] O LEUM GOD, God luk, nga tuku nu yurum tuh kom in karinginyu; Langoeyula ac moliyula lukelos nukewa su ukweyu.
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Kom fin tia, elos ac tulakinyula ac sreyuwi Oana soko lion sulallal, Yen wangin mwet ac fah ku in moliyula.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
O LEUM GOD luk, fin pwaye lah nga oru kutena sin ma inge: Pouk fin oru ma tafongla,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
Ku nga fin orala ma koluk nu sin mwet kawuk luk, Ku kunausla mwet lokoalok luk ke wangin sripa,
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
Na lela mwet lokoalok luk in ukweyu ac sruokyuwi. Lela elos in sisyuwi nu infohk uh ac uniyuwi, Ac filiyuwi ngan oan misa infohk uh.
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
O LEUM GOD, tuyak ke kasrkusrak lom, Ac lain folo lun mwet lokoalok luk! Mukuiyak ac kasreyu! Kom lungsum nununku suwohs,
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
Ke ma inge, orani mwet nukewa nu yurum, Tuh kom in nununkalos lucng me.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Kom pa nununku mwet nukewa. O LEUM GOD, wiyu lac ke kom nununkeyu, Mweyen kom etu lah wangin mwetik.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Kom sie God suwoswos Ac kom nununku nunak lasr ac ma lungse lasr. Kutongya orekma lun mwet koluk Ac sang ma lacne nu sin mwet wo.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
God El mwe loeyuk luk. El molelos su aksol.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
God El oru nununku suwoswos Ac El kwase mwet koluk.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Elos fin tia auliyak, Na God El ac fah tamla cutlass natul, Ac akoela mwe pisr natul.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
El srukak mwe mweun natul Ac ngasla mwe pisr firir natul.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Liye ke mwet koluk elos lungse sramtauk pwapa koluk; Elos purakak lokoalok ac kiapu mwet.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
Tusruktu mwe kwasrip elos akoo nu sin mwet saya, Elos sifacna sremla kac.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Ke ma inge elos akkeokyeyuk ke ma koluk lalos sifacna, Ac akngalyeyuk ke sulallal lalos.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Nga sang kulo nu sin LEUM GOD ke nununku suwohs lal; Nga on ac kaksakin LEUM GOD Fulatlana.

< Masalimo 7 >