< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
Complainte de David, qu'il chanta à l'Éternel à propos de Cus, Benjamite. Éternel, mon Dieu, à toi j'ai mon recours: sauve-moi de tous mes persécuteurs, et me délivre!
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
de peur que, comme un lion, ils ne me déchirent, m'écrasant, faute de libérateur.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Éternel, mon Dieu! si c'est ici ce que j'ai fait, s'il y a de l'iniquité dans mes mains,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
si j'ai payé mon ami par le mal, dépouillé celui qui me haïssait sans cause;
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
que l'ennemi poursuive ma vie, qu'il m'atteigne et me foule contre terre, et traîne ma gloire dans la poussière! (Pause)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Lève-toi, Éternel, dans ta colère! élève-toi contre les fureurs de mes ennemis! Sus! à moi! apprête le jugement!
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
Que l'assemblée des peuples t'environne! au-dessus d'elle monte sur un lieu élevé!
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
L'Éternel juge les peuples: Éternel, fais-moi justice! que selon ma justice et mon innocence il me soit fait!
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Mets donc fin à la malice des impies, et fortifie le juste! toi qui sondes les cœurs et les reins, Dieu juste!
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Mon bouclier est par-devers Dieu, qui est en aide à ceux dont le cœur est droit.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
Dieu est un juste juge, un Dieu prêt à s'irriter en tout temps.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
S'il ne s'arrête, Il aiguise son épée, Il bande son arc et l'ajuste,
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
et dirige sur lui des traits mortels, des traits qu'il enflamme.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Voici, il avait conçu le mal, et portait la malice dans son sein; mais il a enfanté une déception.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
Il a fait une fosse, il l'a creusée, mais il est tombé dans le creux par lui préparé.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Sa malice retombe sur sa tête, et sa violence redescend sur son front.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
J'exalterai l'Éternel selon sa justice, et je chanterai le nom de l'Éternel, du Très-haut.