< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
For the ignoraunce of Dauid, which he songe to the Lord on the wordis of Ethiopien, the sone of Gemyny. Mi Lord God, Y haue hopid in thee; make thou me saaf fro alle that pursuen me, and delyuere thou me.
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Lest ony tyme he as a lioun rauysche my soule; the while noon is that ayenbieth, nether that makith saaf.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Mi Lord God, if Y dide this thing, if wickidnesse is in myn hondis;
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
if Y `yeldide to men yeldynge to me yuels, falle Y `bi disseruyng voide fro myn enemyes;
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
myn enemy pursue my soule, and take, and defoule my lijf in erthe; and brynge my glorie in to dust.
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Lord, rise thou vp in thin ire; and be thou reysid in the coostis of myn enemyes.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
And, my Lord God, rise thou in the comaundement, which thou `hast comaundid; and the synagoge of puplis schal cumpasse thee.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
And for this go thou ayen an hiy; the Lord demeth puplis. Lord, deme thou me bi my riytfulnesse; and bi myn innocence on me.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
The wickidnesse of synneris be endid; and thou, God, sekyng the hertis and reynes, schalt dresse a iust man.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Mi iust help is of the Lord; that makith saaf riytful men in herte.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
The Lord is a iust iuge, stronge and pacient; whether he is wrooth bi alle daies?
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
If ye ben `not conuertid, he schal florische his swerd; he hath bent his bouwe, and made it redi.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
And therynne he hath maad redi the vessels of deth; he hath fulli maad his arewis with brennynge thingis.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Lo! he conseyuede sorewe; he peynfuli brouyte forth vnriytfulnesse, and childide wickidnesse.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
He openide a lake, and diggide it out; and he felde in to the dich which he made.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
His sorewe schal be turned in to his heed; and his wickidnesse schal come doun in to his necke.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
I schal knouleche to the Lord bi his riytfulnesse; and Y schal synge to the name of the hiyeste Lord.