< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
A musical composition of David, which he sang to Yahweh concerning the words of Cush the Benjamite. Yahweh my God, I take refuge in you! Save me from all who chase me, and rescue me.
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Otherwise, they will rip me apart like a lion, tearing me in pieces with no one else able to bring me to safety.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Yahweh my God, if I have done this, and there is guilt on my hands—
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
if I have done evil to him who was at peace with me, or senselessly harmed my enemy without cause, then hear my words.
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
Then let my enemy pursue my life and overtake me; let him trample my life to the ground and lay my honor in the dust. (Selah)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Arise, Yahweh, in your anger; stand up against the rage of my enemies; wake up for my sake and carry out the righteous decrees that you have commanded for them.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
The countries are assembled all around you; take once more your rightful place over them.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Yahweh, judge the nations; vindicate me, Yahweh, because I am righteous and innocent, Most High.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
May the evil deeds of the wicked come to an end, but establish the righteous people, righteous God, you who examine hearts and minds.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
My shield comes from God, the one who saves the upright in heart.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
God is a righteous judge, a God who is indignant each day.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
If a person does not repent, God will sharpen his sword and will prepare his bow for battle.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
He prepares to use weapons against him; he makes his arrows flaming shafts.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Think about the one who is pregnant with wickedness, who conceives destructive plans, who gives birth to harmful lies.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
He digs a pit and hollows it out and then falls into the hole he has made.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
His own destructive plans return to his own head, for his violence comes down on his own head.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
I will give thanks to Yahweh for his justice; I will sing praise to Yahweh Most High.