< Masalimo 7 >

1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
[A meditation by David, which he sang to the LORD, concerning the words of Cush, the Benjamite.] LORD, my God, I take refuge in you. Save me from all those who pursue me, and deliver me,
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
lest they tear apart my soul like a lion, ripping it in pieces, while there is none to deliver.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
LORD, my God, if I have done this, if there is iniquity in my hands,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
if I have rewarded evil to him who was at peace with me, or oppressed my enemy without cause,
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
let the enemy pursue my soul, and overtake it; yes, let him tread my life down to the earth, and lay my glory in the dust. (Selah)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Arise, LORD, in your anger. Lift up yourself against the rage of my adversaries. Awake, my God; you have appointed judgment.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
And let the congregation of the peoples surround you, and rule over them on high.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
The LORD administers judgment to the peoples. Judge me, LORD, according to my righteousness, and to my integrity that is in me.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Oh let the wickedness of the wicked come to an end, but establish the righteous. The righteous God tests hearts and minds.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
My shield is with God, who saves the upright in heart.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
God is a righteous judge, yes, a God who has indignation every day.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
If a man doesn't relent, he will sharpen his sword; he has bent and strung his bow.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
He has also prepared for himself deadly weapons. He makes ready his flaming arrows.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Look, he travails with iniquity. Yes, he has conceived mischief, and brought forth falsehood.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
He has dug a hole, and has fallen into the pit which he made.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
The trouble he causes shall return to his own head, and his violence shall come down on the crown of his own head.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
I will give thanks to the LORD according to his righteousness, and will sing praise to the name of the LORD Most High.

< Masalimo 7 >