< Masalimo 7 >

1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
“A Shiggayon of David, which he sang unto the Lord, concerning the affairs of Cush the Benjamite.” O Lord my God, in thee do I put my trust; save me from every one of my persecutors, and deliver me:
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Lest he tear like a lion my soul, rending it in pieces, with none to deliver.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
O Lord my God, if I have done this; if there be injustice in my hands;
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
If I have recompensed him that was at peace with me with evil; If I have taken aught from my assailants without cause:
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
May the enemy hotly pursue my soul, and overtake it; and tread down upon the earth my life, and cause my honor to be in the dust. (Selah)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Arise, O Lord, in thy anger, lift up thyself because of the rage of my enemies: and awake for me [to] the judgment that thou hast commanded.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
So shall the congregation of nations compass thee about: and for their sakes return thou to the height.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
The Lord will judge the people: judge me, O Lord, according to my righteousness, and according to my integrity [grant] me [recompense].
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Oh let the evil of the wicked come to an end; but establish the just, O thou, who triest the hearts and reins, O righteous God.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
My protection is by God, who saveth the upright in heath.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
God is a righteous judge, and a God who is indignant [with the wicked] every day.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
If he turn not, He will whet his sword, he bendeth his bow, and maketh it ready.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
Also for him he prepareth the instruments of death; he fashioneth his arrows against the persecutors.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Behold, he travaileth with wrong doing; but he hath conceived mischief, and bringeth forth falsehood.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
He hath hollowed out a pit, and dug it, and is fallen into the ditch which he hath wrought.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
His mischief will return upon his own head, and upon his own skull will his violence come down.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
I will thank the Lord according to his righteousness; and I will sing praises to the name of the Lord the Most High.

< Masalimo 7 >