< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
O LORD my God, in you do I put my trust: save me from all them that persecute me, and deliver me:
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Lest he tear my soul like a lion, rending it in pieces, while there is none to deliver.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
O LORD my God, If I have done this; if there be iniquity in my hands;
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
If I have rewarded evil unto him that was at peace with me; (yea, I have delivered him that without cause is mine enemy: )
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
Let the enemy persecute my soul, and take it; yea, let him tread down my life upon the earth, and lay mine honour in the dust. (Selah)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Arise, O LORD, in your anger, lift up yourself because of the rage of mine enemies: and awake for me to the judgment that you have commanded.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
So shall the congregation of the people compass you about: for their sakes therefore return you on high.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
The LORD shall judge the people: judge me, O LORD, according to my righteousness, and according to mine integrity that is in me.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Oh let the wickedness of the wicked come to an end; but establish the just: for the righteous God tries the hearts and reins.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
My defence is of God, which saves the upright in heart.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
God judges the righteous, and God is angry with the wicked every day.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
If he turn not, he will sharpen his sword; he has bent his bow, and made it ready.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
He has also prepared for him the instruments of death; he ordains his arrows against the persecutors.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Behold, he labors with iniquity, and has conceived mischief, and brought forth falsehood.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
He made a pit, and dug it, and is fallen into the ditch which he made.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
His mischief shall return upon his own head, and his violent dealing shall come down upon his own crown of the head.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
I will praise the LORD according to his righteousness: and will sing praise to the name of the LORD most high.