< Masalimo 7 >
1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
En Skiggajon, af David, som han sang for Herren, over Benjaminiten Kus's Ord.
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Herre, min Gud! jeg tror paa dig, frels mig fra alle mine Forfølgere og red mig,
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
at han ikke som en Løve skal slide min Sjæl, ja, rive den bort, uden at der er nogen, som redder.
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
Herre, min Gud! dersom jeg har gjort dette, dersom der er Uret i mine Hænder;
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
dersom jeg har vederlagt den ondt, som holder Fred med mig, — og jeg har dog friet den, som var min Fjende uden Aarsag —;
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
saa forfølge Fjenden min Sjæl og gribe den og nedtræde mit Liv til Jorden og lade min Ære bo i Støvet! (Sela)
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
Staa op, Herre! i din Vrede, hæv dig imod mine Fjenders Forbitrelse, og vaagn op mig til Hjælp; du har beskikket Ret.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Og lad Folkenes Forsamling omringe dig, og op over den vend tilbage til det høje!
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Herren dømmer Folkene; døm mig, Herre! efter min Retfærdighed og efter min Oprigtighed, som er hos mig.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Lad dog de ugudeliges Ondskab faa Ende, men stadfæst den retfærdige, du, som prøver Hjerter og Nyrer, retfærdige Gud!
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
Mit Skjold er hos Gud, som frelser de oprigtige af Hjertet.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Gud er en retfærdig Dommer og en Gud, som vredes hver Dag.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
Dersom de ikke ville omvende sig, da skal han skærpe sit Sværd; han har spændt sin Bue og beredt den;
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
og han har beredt dødelige Vaaben imod dem; sine Pile gør han brændende.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
Se, han undfanger Uret; og han er frugtsommelig med Misgerning og føder Løgn.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Han har gravet en Grav og opkastet den; men han skal falde i Graven, som han gør.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Hans Misgerning skal komme tilbage paa hans Hoved, og hans Voldsfærd skal nedfare paa hans Isse. Jeg vil takke Herren efter hans Retfærdighed og lovsynge Herren den Højestes Navn.