< Masalimo 7 >

1 Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
Osvědčení neviny Davidovy, o čemž zpíval Hospodinu z příčiny slov Chusi syna Jeminova. Hospodine Bože můj, v toběť doufám, vysvoboď mne ode všech protivníků mých, a vytrhni mne,
2 mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
Aby neuchvátil jako lev duše mé, a neroztrhal, když by nebyl, kdo by vysvobodil.
3 Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
Hospodine Bože můj, učinil-li jsem to, jest-li nepravost při mně,
4 ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
Èinil-li jsem zle tomu, kdož se ke mně pokojně choval, (nýbrž spomáhal jsem protivícímu se mi bez příčiny),
5 pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
Nechať stihá nepřítel duši mou, i popadne, a pošlapá na zemi život můj, a slávu mou v prach uvede. (Sélah)
6 Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
Povstaň, Hospodine, v hněvě svém, vyvyš se proti vzteklostem mých nepřátel, a prociť ke mně, nebo jsi soud nařídil.
7 Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
I shrne se k tobě shromáždění lidí; pro ně tedy u výsost navrať se zase.
8 Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
Hospodin souditi bude lidi. Sudiž mne, Hospodine, podlé spravedlnosti mé, a podlé nevinnosti mé, kteráž při mně jest.
9 Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
Ó by již k skončení přišla nešlechetnost bezbožných, spravedlivého pak abys utvrdil ty, kterýž zkušuješ srdce a ledví, Bože spravedlivý.
10 Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
Bůh jest štít můj, kterýž spaseny činí upřímé srdcem.
11 Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
Bůh jest soudce spravedlivý, Bůh silný hněvá se na bezbožného každý den.
12 Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Neobrátí-li se, naostříť meč svůj; lučiště své natáhl, a naměřil je.
13 Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
Připravil sobě i zbroj smrtelnou, střely své proti škůdcím přistrojil.
14 Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
Aj, rodí nepravost; nebo počav těžkou bolest, urodí lež.
15 Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
Jámu kopal, i vykopal ji, ale padne do dolu, kterýž přistrojil.
16 Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
Obrátíť se usilování jeho na hlavu jeho, a na vrch hlavy jeho nepravost jeho sstoupí.
17 Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.
Slaviti budu Hospodina podlé spravedlnosti jeho, a žalmy zpívati jménu Hospodina nejvyššího.

< Masalimo 7 >