< Masalimo 69 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.” Pulumutseni Inu Mulungu, pakuti madzi afika mʼkhosi
Kumqondisi wokuhlabela. Itshuni ethi, “Amaluba.” ElikaDavida. Ngisindisa, Oh Nkulunkulu, ngoba umsinga wamanzi usugamenxe ngentamo yami.
2 Ine ndikumira mʼthope lozama mʼmene mulibe popondapo. Ndalowa mʼmadzi ozama; mafunde andimiza.
Ngiyagalula ezinzikini ezitotayo, lapho okungekho ndawo yokugxila. Sengifike enzikini; impophoma sezingikhulela.
3 Ndafowoka ndikupempha chithandizo; kummero kwanga kwawuma gwaa, mʼmaso mwanga mwada kuyembekezera Mulungu wanga.
Sengidiniwe yikumemeza ngicela uncedo; umphimbo wami usome qha. Amehlo ami aseze efiphele, edinga uNkulunkulu wami.
4 Iwo amene amadana nane popanda chifukwa ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga; ambiri ndi adani anga popanda chifukwa, iwo amene akufunafuna kundiwononga. Ndikukakamizidwa kubwezera zomwe sindinabe.
Labo abangizondayo kungelasizatho banengi okwedlula inwele zekhanda lami; banengi abayizitha zami kungelambangela, labo abafuna ukungidiliza. Ngiyaphoqelwa ukuhlawula engingakuntshontshanga.
5 Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu, kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.
Uyabazi ubuthutha bami, wena Nkulunkulu; isono sami kasifihlakalanga kuwe.
6 Iwo amene amadalira Inu asanyozedwe chifukwa cha ine, Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Iwo amene amafunafuna Inu asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine, Inu Mulungu wa Israeli.
Akuthi labo abathemba kuwe bangayangiswa ngenxa yami, Oh Thixo, Thixo Somandla; akuthi labo abakudingayo, bangahlaziswa ngenxa yami, Oh Nkulunkulu ka-Israyeli.
7 Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu, ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.
Ngiyakubhensela ukugconwa ngenxa yakho, ihlazo lihuqiwe ebusweni bami.
8 Ndine mlendo kwa abale anga, munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;
Ngingowemzini kubafowethu, ngingowemzini emadodaneni kamama;
9 pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.
ngoba ukutshisekela indlu yakho kufuthelene kimi, lezethuko zalabo abakuthukayo ziwela kimi.
10 Pamene ndikulira ndi kusala kudya, ndiyenera kupirira kunyozedwa;
Ngithi lapho ngilila ngizila ukudla, ngibhensele ukwetheswa inhlamba;
11 pomwe ndavala chiguduli, anthu amandiseweretsa.
kuthi lapho ngivunula amasaka abantu badlale ngami.
12 Iwo amene amakhala pa chipata amandinena, ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.
Labo abalinda emasangweni bayangihleka, ngiyingoma nje yezidakwa.
13 Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye, pa nthawi yanu yondikomera mtima; mwa chikondi chanu chachikulu Inu Mulungu, mundiyankhe pondipulumutsa.
Kodwa ngikhuleka kuwe, Oh Thixo, ngesikhathi somusa wakho; ngothando lwakho olukhulu, Oh Nkulunkulu, ngiphendula ngensindiso yakho eqinisekileyo.
14 Mundilanditse kuchoka mʼmatope, musalole kuti ndimire, pulumutseni ine kwa iwo amene amadana nane, kuchoka mʼmadzi ozama.
Ngihlenga exhaphozini, ungangiyekeli ngigalule; ngikhulula kulabo abangizondayo, emanzini atshonayo.
15 Musalole kuti chigumula chindimeze, kuya kusandimeze ndipo dzenje lisatseke pakamwa pake kundimiza.
Ungayekeli izikhukhula zingigalulise loba inziki zingiginye, loba umgodi uvaleke umlomo wawo phezu kwami.
16 Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu; mwa chifundo chanu chachikulu tembenukirani kwa ine.
Ngiphendula, Oh Thixo, ngenxa yokulunga kothando lwakho; emuseni wakho omkhulu phendukela kimi.
17 Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu, ndiyankheni msanga, pakuti ndili pa mavuto.
Ungayifihleli ubuso bakho inceku yakho; ngiphendula masinyane, ngoba ngiphakathi kohlupho.
18 Bwerani pafupi ndi kundilanditsa; ndiwomboleni chifukwa cha adani anga.
Sondela ungikhulule; ngihlenga ngenxa yezitha zami.
19 Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera, kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu.
Uyakwazi ukuthi ngigconwa njani, ngihlaziswa njalo ngiyangiswa; zonke izitha zami ziphambi kwakho.
20 Mnyozo waswa mtima wanga ndipo wandisiya wopanda thandizo lililonse; ndinafunafuna ena woti andichitire chisoni, koma panalibe ndi mmodzi yemwe woti anditonthoze, sindinapeze ndi mmodzi yemwe.
Ukugconwa sekuyephule inhliziyo yami kwangitshiya esithubeni; ngadinga uzwelo ngaluswela, abaduduzi, kodwa ngabaswela.
21 Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa ndi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu.
Bathela inyongo ekudleni kwami banginathisa iviniga nxa ngomile.
22 Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha; chikhale chobwezera chilango ndiponso khwekhwe.
Sengathi itafula eliphambi kwabo lingaba ngumjibila; sengathi lingaba yisijeziso lesithiyo.
23 Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso ndipo misana yawo ipindike mpaka kalekale.
Sengathi amehlo abo angafiphala ukuze bangaboni, lamaqolo abo akhokhobe kokuphela.
24 Khuthulirani ukali wanu pa iwo; mkwiyo wanu woyaka moto uwathe mphamvu.
Thululela ulaka lwakho phezu kwabo; akuthi ulaka lwakho olwesabekayo lubehlele.
25 Malo awo akhale wopanda anthu pasapezeke ndi mmodzi yemwe wokhala mʼmatenti awo.
Sengathi indawo yabo ingaba ngamanxiwa; akungabi lamuntu ozahlala emathenteni abo.
26 Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulaza ndi kuyankhula zowawa kwa amene munawapweteka.
Ngoba bahlupha labo obalimazayo bakhulume ngobuhlungu balabo obalimazayo.
27 Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo, musalole kuti akhale ndi gawo pa chipulumutso chanu.
Bethese amacala phezu kwamacala; ungayekeli bazuze isabelo sensindiso yakho.
28 Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyo ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama.
Sengathi bangesulwa encwadini yokuphila bangaze babalwa kanye labalungileyo.
29 Ndikumva zowawa ndi kuzunzika; lolani chipulumutso chanu, Inu Mulungu, chinditeteze.
Ngisebuhlungwini, ngikhathazekile; sengathi insindiso yakho, Oh Nkulunkulu ingangivikela.
30 Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo, ndidzalemekeza Iye ndi chiyamiko.
Ngizalidumisa ibizo likaNkulunkulu ngengoma, ngilibabaze ngokubonga.
31 Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe, kupambananso ngʼombe yayimuna, pamodzi ndi nyanga ndi ziboda zake.
Lokhu kuzamthabisa uThixo okwedlula inkabi, okwedlula inkunzi yonke ilempondo lamangqina ayo.
32 Wosauka adzaona ndipo adzasangalala, Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo!
Abayanga bazabona bajabule lina elimdingayo uNkulunkulu, sengathi inhliziyo zenu zingaphila!
33 Yehova amamvera anthu osowa ndipo sanyoza anthu ake omangidwa.
UThixo uyabezwa abaswelayo, kabeyisi abantu bakhe abathunjiweyo.
34 Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye, nyanja ndi zonse zomwe zimayenda mʼmenemo,
Akuthi izulu lomhlaba kumdumise, inlwandle lakho konke okunyakaza kuzo,
35 pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni ndi kumanganso mizinda ya Yuda, anthu adzakhala kumeneko ndipo dzikolo lidzakhala lawo;
ngoba uNkulunkulu uzayisindisa iZiyoni ayakhe kutsha imizi yakoJuda. Yikhona-ke abantu bazakwakha khona balithathe libe ngelabo;
36 ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo, ndipo iwo amene amakonda dzina lake adzakhala kumeneko.
abantwana bezinceku zayo lizakuba yilifa labo, labalithandayo ibizo lakhe bazahlala khona.

< Masalimo 69 >