< Masalimo 68 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
UNkulunkulu kavuke, zihlakazeke izitha zakhe, labamzondayo babaleke phambi kwakhe.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
Njengokuphetshethwa kwentuthu baphephethe; njengokuncibilikiswa kwengcino phambi komlilo, ababi kabachithwe phambi kukaNkulunkulu.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
Kodwa abalungileyo kabajabule, bathabe phambi kukaNkulunkulu, njalo bathokoze ngentokozo.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Hlabelelani kuNkulunkulu, hlabelelani indumiso ebizweni lakhe, limphakamise lowo ogade esedlula emagcekeni enkangala ngebizo lakhe uJehova, njalo thokozani phambi kwakhe.
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
Unguyise wezintandane lomahluleli wabafelokazi, uNkulunkulu endaweni yakhe yokuhlala engcwele.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
UNkulunkulu uhlalisa ababodwa emulini, ukhupha ababotshiweyo ebasa empumelelweni, kodwa abalenkani bahlala elizweni elomileyo.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
Nkulunkulu, ekuphumeni kwakho phambi kwabantu bakho, ekuhambeni kwakho enkangala; (Sela)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
Umhlaba wazamazama, lawo amazulu athontisa phambi kukaNkulunkulu, le iSinayi, phambi kukaNkulunkulu, uNkulunkulu kaIsrayeli.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
Walinisa izulu elikhulu, Nkulunkulu; waliqinisa wena ilifa lakho selikhathele.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Ibandla lakho lahlala kulo; wamlungisela ngobuhle bakho oswelayo, Nkulunkulu.
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
INkosi yanika ilizwi; abesifazana ababika izindaba babelixuku elikhulu.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
Amakhosi amabutho ayabaleka, ayabaleka. Owesifazana ohlezi ekhaya wayaba impango.
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
Lanxa lilala phakathi kwezibaya zezimvu, lizakuba njengempiko zejuba ezisitshekelwe ngesiliva, lezinsiba zalo ngegolide eliliganu.
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
Lapho uSomandla echitha amakhosi kulo, kwaba mhlophe njengeliqhwa elikhithikileyo eZalimoni.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
Intaba yeBashani yintaba kaNkulunkulu, intaba elezingqonga, intaba yeBashani.
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Likhangelelani ngomhawu, lina zintaba zezingqonga? Lintaba uNkulunkulu uyiloyisele ukuhlala kwakhe. Yebo, iNkosi izahlala kuyo kuze kube nininini.
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
Izinqola zikaNkulunkulu ziyizinkulungwane ezingamatshumi amabili, izinkulungwane zezinkulungwane, iNkosi iphakathi kwazo, iSinayi endaweni engcwele.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
Wena wenyukele phezulu, wathumba abathunjiweyo; wemukela izipho ebantwini, yebo, lakwabalenkani; ukuze uJehova uNkulunkulu ahlale khona.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Kayibongwe iNkosi; isethwesa insuku ngensuku; uNkulunkulu ulusindiso lwethu. (Sela)
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
UNkulunkulu wethu unguNkulunkulu wezinsindiso; lakuJehova iNkosi kulokuphuma ekufeni.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
Kodwa uNkulunkulu uzaphohloza ikhanda lezitha zakhe, ukhakhayi olulenwele lwalowo ohamba ezonweni zakhe.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
INkosi yathi: Ngizababuyisa bevela eBashani, ngibabuyise bevela enzikini yolwandle,
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
ukuze inyawo zakho uzigxamuze egazini lezitha, inlimi zezinja zakho kulo.
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
Zibonile izindwendwe zakho, Nkulunkulu; izindwendwe zikaNkulunkulu wami, iNkosi yami, endaweni engcwele.
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
Ngaphambili kuhamba abahlabelayo, ngemuva abatshayi bamachacho, phakathi izintombi zitshaya izigubhu.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
Bongani uNkulunkulu emabandleni, iNkosi, kuvela emthonjeni kaIsrayeli.
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
Nango uBhenjamini omncinyane umbusi wabo, iziphathamandla zikaJuda, inkundla yazo, iziphathamandla zikaZebuluni, iziphathamandla zikaNafithali.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
UNkulunkulu wakho ulaye amandla akho; qinisa, Nkulunkulu, lokho osenzele khona.
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
Ngenxa yethempeli lakho eJerusalema amakhosi azakulethela isipho.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Sikhuze isilo somhlanga, umhlambi wezinkunzi kanye lamankonyana abantu, kuze kuthobeke kulenhlamvu zesiliva; ubahlakaze abantu abathokoza ezimpini.
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
Iziphathamandla zizakuza zivela eGibhithe; iEthiyophiya izakwelulela izandla zayo kuNkulunkulu ngokuphangisa.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
Mibuso yomhlaba, hlabelelani kuNkulunkulu, lihlabelele indumiso eNkosini. (Sela)
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
Kuyo egade phezu kwamazulu amazulu awendulo; khangelani, iphumisa ilizwi layo, ilizwi elilamandla.
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Phanini amandla kuNkulunkulu; ubukhosi bakhe buphezu kukaIsrayeli, lamandla akhe asemayezini.
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
Uyesabeka, Nkulunkulu, ezindaweni zakho ezingcwele; uNkulunkulu kaIsrayeli nguye onika abantu bakhe amandla lengalo. Kabongwe uNkulunkulu.

< Masalimo 68 >