< Masalimo 68 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
“For the leader of the music. A psalm of David.” Let God arise, and his enemies are scattered, And they who hate him flee before him!
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
As smoke is dispersed, so thou dispersest them; As wax melteth before the fire, So perish the wicked before the face of God.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
But the righteous are glad and rejoice in his presence, Yea, they exult exceedingly.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Sing unto God; sing praises to his name! Prepare a way for him who rideth through the desert! Jehovah is his name; be joyful in his presence!
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
The father of the fatherless, and the protector of the widow, Is God in his holy habitation.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
God causeth the forsaken to dwell in houses; He leadeth forth to prosperity them that are bound; But the rebellious shall dwell in a barren land.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
O God! when thou didst go before thy people, When thou didst march through the wilderness. (Pause)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
The earth quaked, and the heavens dropped at the presence of God; This Sinai trembled at the presence of God, the God of Israel.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
Thou, O God! didst send a plentiful rain; Thou didst strengthen thy wearied inheritance.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Thy people established themselves in the land; Thou, O God! in thy goodness, didst prepare it for the needy!
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
The Lord gave the song of victory Of the maidens publishing glad tidings to the mighty host.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
“The kings with their armies have fled, —have fled! And the matron at home divideth the spoil.
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
Truly ye may repose yourselves in the stalls, Like the wings of a dove covered with silver, And her feathers with shining gold.”
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
When the Most High destroyed the kings in the land, It was white [[with their bones]] like Salmon.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
Ye lofty hills, ye hills of Bashan, Ye many-topped hills, ye hills of Bashan,
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Why frown ye, ye many-topped hills, At the hill in which God is pleased to dwell, In which Jehovah will dwell for ever?
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
The chariots of God are myriads, yea, thousands of thousands; The Lord is in the midst of them, as upon Sinai, in the sanctuary.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
Thou hast ascended on high, Thou hast led captive the vanquished, Thou hast received gifts among men, Even the rebellious, that here thou mightst dwell, O LORD God!
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Praised be the Lord daily! When we are heavy-laden, the Mighty One is our help.
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
Our God is a God of salvation; From the Lord Jehovah cometh deliverance from death.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
But God smiteth the head of his enemies, Even the hairy crowns of those who go on in their iniquity.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
“I will bring them back,” saith the Lord, “from Bashan; I will bring them back from the deep sea;
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
That thy foot may be dipped in their blood, That thy dogs may drink the blood of thine enemies.”
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
We have seen thy procession, O God! The procession of my God, my king, to his sanctuary!
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
The singers go before, the minstrels follow, Amidst damsels playing on timbrels.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
Praise ye God in your assemblies; Praise the Lord, all ye from the fountain of Israel!
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
Here is Benjamin, the youngest, and his leaders; The chiefs of Judah, and their band; The chiefs of Zebulon, and the chiefs of Naphtali.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
Thy God has ordained thy strength, [[O Israel!]] Show forth thy might, O God! thou who hast wrought for us!
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
Because of thy temple in Jerusalem Shall kings bring presents to thee.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Rebuke the wild beast of the reeds, The multitude of bulls with the calves of the nations, So that they shall cast themselves down with masses of silver; Scatter thou the nations that delight in war!
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
Princes shall come out of Egypt; Ethiopia shall haste with outstretched hands to God.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
Ye kingdoms of the earth, sing unto God; Sing praises to Jehovah;
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
To him who rideth upon the ancient heaven of heavens! Behold, he uttereth his voice, his mighty voice!
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Give glory to God, Whose majesty is in Israel, and whose might is in the clouds!
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
Terrible art thou, O God! from thy sanctuary! The God of Israel giveth strength and power to his people. Praised be God!

< Masalimo 68 >