< Masalimo 68 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
For the Leader. A Psalm of David, a Song. Let God arise, let His enemies be scattered; and let them that hate Him flee before Him.
2 Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
As smoke is driven away, so drive them away; as wax melteth before the fire, so let the wicked perish at the presence of God.
3 Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
But let the righteous be glad, let them exult before God; yea, let them rejoice with gladness.
4 Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
Sing unto God, sing praises to His name; extol Him that rideth upon the skies, whose name is the LORD; and exult ye before Him.
5 Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
A father of the fatherless, and a judge of the widows, is God in His holy habitation.
6 Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
God maketh the solitary to dwell in a house; He bringeth out the prisoners into prosperity; the rebellious dwell but in a parched land.
7 Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
O God, when Thou wentest forth before Thy people, when Thou didst march through the wilderness; (Selah)
8 dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
The earth trembled, the heavens also dropped at the presence of God; even yon Sinai trembled at the presence of God, the God of Israel.
9 Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
A bounteous rain didst Thou pour down, O God; when Thine inheritance was weary, Thou didst confirm it.
10 Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
Thy flock settled therein; Thou didst prepare in Thy goodness for the poor, O God.
11 Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
The Lord giveth the word; the women that proclaim the tidings are a great host.
12 “Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
Kings of armies flee, they flee; and she that tarrieth at home divideth the spoil.
13 Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
When ye lie among the sheepfolds, the wings of the dove are covered with silver, and her pinions with the shimmer of gold.
14 Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
When the Almighty scattereth kings therein, it snoweth in Zalmon.
15 Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
A mountain of God is the mountain of Bashan; a mountain of peaks is the mountain of Bashan.
16 Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
Why look ye askance, ye mountains of peaks, at the mountain which God hath desired for His abode? Yea, the LORD will dwell therein for ever.
17 Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
The chariots of God are myriads, even thousands upon thousands; the Lord is among them, as in Sinai, in holiness.
18 Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
Thou hast ascended on high, Thou hast led captivity captive; Thou hast received gifts among men, yea, among the rebellious also, that the LORD God might dwell there.
19 Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
Blessed be the Lord, day by day He beareth our burden, even the God who is our salvation. (Selah)
20 Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
God is unto us a God of deliverances; and unto GOD the Lord belong the issues of death.
21 Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
Surely God will smite through the head of His enemies, the hairy scalp of him that goeth about in his guiltiness.
22 Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
The Lord said: 'I will bring back from Bashan, I will bring them back from the depths of the sea;
23 Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
That thy foot may wade through blood, that the tongue of thy dogs may have its portion from thine enemies.'
24 Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
They see Thy goings, O God, even the goings of my God, my King, in holiness.
25 Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
The singers go before, the minstrels follow after, in the midst of damsels playing upon timbrels.
26 Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
'Bless ye God in full assemblies, even the Lord, ye that are from the fountain of Israel.'
27 Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
There is Benjamin, the youngest, ruling them, the princes of Judah their council, the princes of Zebulun, the princes of Naphtali.
28 Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
Thy God hath commanded thy strength; be strong, O God, Thou that hast wrought for us
29 Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
Out of Thy temple at Jerusalem, whither kings shall bring presents unto Thee.
30 Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
Rebuke the wild beast of the reeds, the multitude of the bulls, with the calves of the peoples, every one submitting himself with pieces of silver; He hath scattered the peoples that delight in war!
31 Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
Nobles shall come out of Egypt; Ethiopia shall hasten to stretch out her hands unto God.
32 Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
Sing unto God, ye kingdoms of the earth; O sing praises unto the Lord; (Selah)
33 Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
To Him that rideth upon the heavens of heavens, which are of old; lo, He uttereth His voice, a mighty voice.
34 Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
Ascribe ye strength unto God; His majesty is over Israel, and His strength is in the skies.
35 Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!
Awful is God out of thy holy places; the God of Israel, He giveth strength and power unto the people; blessed be God.