< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Mungu atuhurumie sisi na kutubariki na kufanya nuru ya uso wake ituangazie (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
ili kwamba njia zako zijulikane nchi yote, wokovu wako kati ya mataifa yote.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Watu wakusifu wewe, Mungu; watu wote wakusifu wewe.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Oh, mataifa wafurahi na na kuimba kwa furaha, maana utawahukumu watu kwa haki na kuwaongoza mataifa walioko duniani.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Watu wakushukuru wewe, Mungu; watu wote wakusifu wewe.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
Nchi imetoa mavuno yake na Mungu, Mungu wetu, ametubariki.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Mungu ametubariki sisi, na miisho yote ya dunia itamuheshimu yeye.

< Masalimo 67 >