< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Para el director del coro. Un salmo. Un canto. Para acompañamiento con instrumentos de cuerda. Que Dios sea misericordioso con nosotros y nos bendiga. Que hallemos gracia ante sus ojos. (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
Que todos los habitantes de la tierra conozcan tus caminos y tu salvación en medio de todos los pueblos.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Que todos te alaben, Dios. Sí, que todas las naciones te alaben.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Que todos se alegren y canten de gozo porque tú haces juicio justo, y guías a todos los habitantes de la tierra. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Que todos te alaben, Dios. Sí, que todas las naciones te alaben.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
La tierra ha producido su cosecha; y Dios, nuestro Dios, nos ha bendecido.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Dios nos bendecirá, y todos los habitantes de la tierra lo respetarán.

< Masalimo 67 >