< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
برای سالار مغنیان. مزمور و سرود برذوات اوتار خدا بر ما رحم کند و ما را مبارک سازدو نور روی خود را بر ما متجلی فرماید! سلاه.۱
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
تا راه تو در جهان معروف گردد و نجات تو به جمیع امت‌ها.۲
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
‌ای خدا قوم‌ها تو را حمدگویند. جمیع قوم‌ها تو را حمد گویند.۳
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
امت‌ها شادی و ترنم خواهند نمود زیراقوم‌ها را به انصاف حکم خواهی نمود و امت های جهان را هدایت خواهی کرد، سلاه.۴
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
‌ای خداقوم‌ها تو را حمد گویند. جمیع قوم‌ها تو را حمدگویند.۵
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
آنگاه زمین محصول خود را خواهد دادو خدا خدای ما، ما را مبارک خواهد فرمود.۶
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
خداما را مبارک خواهد فرمود. و تمامی اقصای جهان از او خواهند ترسید.۷

< Masalimo 67 >