< Masalimo 67 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Toe hasoan’ Añahare tika naho tahie’e, kinokinohe’e amantika i lahara’ey, Selà
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
Ho fohineñe an-tane atoy o lala’oo, amo kilakila ‘ndatio ty fandrombaha’o.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Ho renge’ ondatio irehe ry Andrianañahare; hene handrenge Azo ondatio.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Hifalea’ o fifeheañeo naho hisaboe’iereo an-kaehake; fa ho zakae’o ami’ty hiti’e ondatio, vaho hiaoloa’o o fifeheañe an-tane atoio. Selà
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Ho renge’ ondatio irehe ry Andrianañahare; fonga handrenge Azo ondatio.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
Fa nahatoly sabo ty tane, nitahy antika t’i Andrianañahare, i Andrianañaharen-tikañey.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Tahien’ Añahare tikañe; soa te hañeveñe ama’e ze hene olon-tane.