< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Kaassian ken bendissionannatayo koma iti Dios ken pagraniagenna ti rupana kadatayo (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
tapno maipakaammo koma dagiti wagasmo iti rabaw ti daga, ti panangisalakanmo kadagiti amin a nasion.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Idaydayawdaka koma, O Dios; idaydayawdaka koma dagiti amin a tattao.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
O, agragsak ken agkanta koma sirarag-o dagiti nasion, ta ukomemto dagiti tattao iti patas ken iturayam dagiti nasion iti rabaw ti daga. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Idaydayawdaka koma, O Dios; idaydayawdaka koma dagiti amin a tattao.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
Pinataud ti daga ti apitna ken binendisionannatayo iti Dios.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Benendisionannatayo ti Dios, ken idaydayaw isuna ti amin a suli ti daga.

< Masalimo 67 >