< Masalimo 67 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Dans les hymnes, psaume d’un cantique de David. Que Dieu ait pitié de nous, et qu’il nous bénisse; qu’il fasse briller la lumière de son visage sur nous, et qu’il ait pitié de nous.
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
Afin que nous connaissions sur la terre votre voie, et votre salut dans toutes les nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Que les peuples vous glorifient, ô Dieu, que tous les peuples vous glorifient.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Que les nations se réjouissent et exultent, parce que vous jugez les peuples avec équité, et que vous dirigez les nations sur la terre.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Que les peuples vous glorifient, ô Dieu, que tous les peuples vous glorifient.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
La terre a donné son fruit. Qu’il nous bénisse, Dieu, notre Dieu,
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Qu’il nous bénisse, Dieu; et que toutes les extrémités de la terre le redoutent.