< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Al la ĥorestro. Por kordaj instrumentoj. Psalmo-kanto. Dio nin korfavoru kaj benu; Li aperigu al ni Sian luman vizaĝon. (Sela)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
Oni ekkonu sur la tero Vian vojon, En ĉiuj popoloj Vian savon.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Danku Vin popoloj, ho Dio, Danku Vin ĉiuj popoloj.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Ĝoju kaj kantu gentoj, Ĉar Vi juĝas popolojn juste, Kaj gentojn sur la tero Vi regas. (Sela)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Danku Vin popoloj, ho Dio, Danku Vin ĉiuj popoloj.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
La tero donis sian frukton; Benos nin Dio, nia Dio.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Benos nin Dio; Kaj respektu Lin ĉiuj limoj de la tero.

< Masalimo 67 >