< Masalimo 67 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
For the Chief Musician. With stringed instruments. A Psalm. A song. May God be merciful to us, bless us, and cause his face to shine on us. (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
That your way may be known on earth, and your salvation among all nations,
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
let the peoples praise you, God. Let all the peoples praise you.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Oh let the nations be glad and sing for joy, for you will judge the peoples with equity, and govern the nations on earth. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise you, God. Let all the peoples praise you.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
The earth has yielded its increase. God, even our own God, will bless us.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
God will bless us. All the ends of the earth shall fear him.