< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
Unto the end. With hymns, a Canticle Psalm of David. May God have mercy on us and bless us. May he shine his countenance upon us, and may he have mercy on us.
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
So may we know your way upon the earth, your salvation among all nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples confess to you, O God. Let all the peoples confess to you.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
May the nations rejoice and exult. For you judge the peoples with equity, and you direct the nations on earth.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples confess to you, O God. Let all the peoples confess to you.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
The earth has provided her fruit. May God, our God, bless us.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
May God bless us, and may all the ends of the earth fear him.

< Masalimo 67 >