< Masalimo 67 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
For the choirmaster. With stringed instruments. A Psalm. A song. May God be gracious to us and bless us, and cause His face to shine upon us,
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
that Your ways may be known on earth, Your salvation among all nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise You, O God; let all the peoples praise You.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Let the nations be glad and sing for joy, for You judge the peoples justly and lead the nations of the earth.
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise You, O God; let all the peoples praise You.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
The earth has yielded its harvest; God, our God, blesses us.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
God blesses us, that all the ends of the earth shall fear Him.