< Masalimo 67 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
For the Chief Musician; on stringed instruments. A Psalm, a Song. God be merciful unto us, and bless us, [And] cause his face to shine upon us; (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
That thy way may be known upon earth, Thy salvation among all nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise thee, O God; Let all the peoples praise thee.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Oh let the nations be glad and sing for joy; For thou wilt judge the peoples with equity, And govern the nations upon earth. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the peoples praise thee, O God; Let all the peoples praise thee.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
The earth hath yielded its increase: God, even our own God, will bless us.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
God will bless us; And all the ends of the earth shall fear him.