< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Müzik şefi için - İlahi - Mezmur Ey yeryüzündeki bütün insanlar, Tanrı'ya sevinç çığlıkları atın!
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Adının yüceliğine ilahiler söyleyin, O'na görkemli övgüler sunun!
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
“Ne müthiş işlerin var!” deyin Tanrı'ya, “Öyle büyük gücün var ki, Düşmanların eğiliyor önünde.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Bütün yeryüzü sana tapınıyor, İlahiler okuyor, adını ilahilerle övüyor.” (Sela)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Gelin, bakın Tanrı'nın neler yaptığına! Ne müthiş işler yaptı insanlar arasında:
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Denizi karaya çevirdi, Atalarımız yaya geçtiler ırmaktan. Yaptığına sevindik orada.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Kudretiyle sonsuza dek egemenlik sürer, Gözleri ulusları süzer; Başkaldıranlar gurura kapılmasın! (Sela)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Ey halklar, Tanrımız'a şükredin, Övgülerini duyurun.
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Hayatımızı koruyan, Ayaklarımızın kaymasına izin vermeyen O'dur.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Sen bizi sınadın, ey Tanrı, Gümüş arıtır gibi arıttın.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Ağa düşürdün bizi, Sırtımıza ağır yük vurdun.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
İnsanları başımıza çıkardın, Ateşten, sudan geçtik. Ama sonra bizi bolluğa kavuşturdun.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Yakmalık sunularla evine gireceğim, Adaklarımı yerine getireceğim,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Sıkıntı içindeyken dudaklarımdan dökülen, Ağzımdan çıkan adakları.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Yakılan koçların dumanıyla semiz hayvanlardan Sana yakmalık sunular sunacağım, Tekeler, sığırlar kurban edeceğim. (Sela)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Gelin, dinleyin, ey sizler, Tanrı'dan korkanlar, Benim için neler yaptığını size anlatayım.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Ağzımla O'na yakardım, Övgüsü dilimden düşmedi.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Yüreğimde kötülüğe yer verseydim, Rab beni dinlemezdi.
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Oysa Tanrı dinledi beni, Kulak verdi duamın sesine.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Övgüler olsun Tanrı'ya, Çünkü duamı geri çevirmedi, Sevgisini benden esirgemedi.

< Masalimo 66 >