< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Načelniku godbe, pesem in psalm. Ukajte Bogu, vsi zemljani.
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Prepevajte slavo njegovega imena; slavo pridevajte hvali njegovi.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Govorite Bogu: Kako čestitljiv si v delih svojih: zavoljo obilosti moči tvoje se ti lažnjivo udajajo sovražniki tvoji.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Vsi zemljani naj se ti klanjajo in ti prepevajo; prepevajo naj tvojemu imenu, presilno.
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Pridite in glejte dela Božja; čestitljiv je v dejanji proti sinovom človeškim.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Morje izpreminja v suho; reko so pregazile noge, tam smo radovali se v njem.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Z močjo svojo gospoduje vekomaj; oči njegove gledajo narode: kateri so uporni, naj se ne povišujejo preveč pri sebi!
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Blagoslavljajte Boga našega, ljudstva, in glas hvale njegove naj se razlega;
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Kateri je dušo našo nazaj postavil v življenje, in ne pripusti, da omahnejo noge naše.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Potem, ko si nas izkušal, Bog, raztopil si nas, kakor se topi srebro.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Peljal si nas v samo mrežo; dél si nam podprsnico okolo ledja.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Storil si, da je sédel človek na glavo našo, šli smo skozi ogenj in skozi vodo; slednjič si nas pripeljal do té sitosti.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Sè žgalnimi darovi pojdem v hišo tvojo in opravim svoje obljube,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Katere so izrekle odprte ustne moje, in govorila moja usta v stiski moji.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Žgalne darí tolstih ovnov bodem ti daroval s kadilom; pripravil vole s kozli, močno.
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Pridite, poslušajte, kateri koli se bojite Boga, da povem, kaj je storil duši moji.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Njega sem klical sè svojimi usti, in povišan sem bil za govore svojega jezika.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Ako bi se bil v krivico obrnil sè srcem svojim, Gospod bi ne bil slišal.
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Ali vendar slišal je Bog, ozrl se v prošnje moje glas.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Blagoslovljen Bog, kateri ni zavrgel prošnje moje in mi ni odtegnil milosti svoje.

< Masalimo 66 >