< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Cântico e salmo para o regente: Gritai de alegria a Deus toda a terra.
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Cantai a glória do nome dele; reconhecei a glória de seu louvor.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Dizei a Deus: Tu [és] temível [em] tuas obras; pela grandeza de tua força os teus inimigos se sujeitarão a ti.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Toda a terra te adorará, e cantará a ti; cantarão ao teu nome. (Selá)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Vinde, e vede os atos de Deus; a obra dele é temível aos filhos dos homens.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Ele fez o mar ficar seco, passaram o rio a pé; ali nos alegramos nele.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Ele governa com seu poder para sempre; seus olhos vigiam as nações; não se exaltem os rebeldes. (Selá)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Vós povos, bendizei a nosso Deus, e fazei ouvir a voz do louvor a ele,
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Que conserva nossas almas em vida, e não permite que nossos pés se abalem.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Porque tu, Deus, tem nos provado; tu nos refinas como se refina a prata.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Tu nos levaste a uma rede; prendeste-nos em nossas cinturas.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Fizeste um homem cavalgar sobre nossas cabeças; passamos pelo fogo e pela água, porém tu nos tiraste para um [lugar] confortável.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Entrarei em tua casa com holocaustos; pagarei a ti os meus votos,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Que meus lábios pronunciaram, e minha boca falou, quando eu estava angustiado.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Eu te oferecerei holocaustos de animais gordos, com incenso de carneiros; prepararei bois com bodes. (Selá)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Vinde, ouvi, todos vós que temeis a Deus, e eu contarei o que ele fez à minha alma.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Clamei a ele com minha boca, e ele foi exaltado pela minha língua.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Se eu tivesse dado valor para a maldade em meu coração, o Senhor não teria [me] ouvido.
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Mas certamente Deus [me] ouviu; ele prestou atenção à voz de minha oração.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Bendito seja Deus, que não ignorou minha oração, nem sua bondade [se desviou] de mim.

< Masalimo 66 >