< Masalimo 66 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Jubilae a Deus, todas as terras.
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Cantae a gloria do seu nome; dae gloria ao seu louvor.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Dizei a Deus: Quão terrivel és tu nas tuas obras! pela grandeza do teu poder se submetterão a ti os teus inimigos.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Toda a terra te adorará e te cantará louvores: elles cantarão o teu nome (Selah)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Vinde, e vêde as obras de Deus: é terrivel nos seus feitos para com os filhos dos homens.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Converteu o mar em terra secca; passaram o rio a pé; ali nos alegrámos n'elle.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Elle domina eternamente pelo seu poder: os seus olhos estão sobre as nações; não se exaltem os rebeldes (Selah)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Bemdizei, povos, ao nosso Deus, e fazei ouvir a voz do seu louvor:
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Ao que sustenta com vida a nossa alma, e não consente que sejam abalados os nossos pés.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Pois tu, ó Deus, nos provaste; tu nos afinaste como se afina a prata.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Tu nos metteste na rede; affligiste os nossos lombos.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Fizeste com que os homens cavalgassem sobre as nossas cabeças; passámos pelo fogo e pela agua; mas nos trouxeste a um logar copioso.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Entrarei em tua casa com holocaustos; pagar-te-hei os meus votos.
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Os quaes pronunciaram os meus labios, e fallou a minha bocca, quando estava na angustia.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Offerecer-te-hei holocaustos gordurosos com incenso de carneiros; offerecerei novilhos com cabritos (Selah)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Vinde, e ouvi, todos os que temeis a Deus, e eu contarei o que elle tem feito á minha alma.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
A elle clamei com a minha bocca, e elle foi exaltado pela minha lingua.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Se eu attender á iniquidade no meu coração, o Senhor não me ouvirá;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Mas, na verdade, Deus me ouviu; attendeu á voz da minha oração.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Bemdito seja Deus, que não rejeitou a minha oração, nem desviou de mim a sua misericordia.