< Masalimo 66 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Kumqondisi wokuhlabela. Ingoma. Ihubo. Memezani ngentokozo kuNkulunkulu mhlaba wonke!
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Hlabelani ngobukhosi bebizo lakhe; yenzani udumo lwakhe lube lenkazimulo!
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Yitshoni kuNkulunkulu lithi, “Imangalisa kangaka imisebenzi yakho! Izitha Zakho ziyethuka phambi Kwakho
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Umhlaba wonke uyakhothama Kuwe; bahlabela udumo Kuwe, bahlabelela udumo ebizweni Lakho.”
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Wozani libone akwenzileyo uNkulunkulu, ukumangalisa kwemisebenzi yakhe ayenzela abantu!
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Waguqula ulwandle lwaba ngumhlabathi owomileyo, badabula phakathi kwamanzi behamba ngezinyawo wozani sithokoze Kuye.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Uyabusa laphakade ngamandla Akhe, amehlo Akhe ayazikhangela izizwe sengathi abahlamuki.
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Dumisani uNkulunkulu wethu, lina bantu lonke, akuthi inhlokomo yokudunyiswa kwakhe izwakale;
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
uzilondolozile impilo zethu wavikela inyawo zethu ukuze zingatsheleli.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Ngoba wena, Oh Nkulunkulu, wasilinga; wasicenga njengesiliva.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Wasingenisa entolongweni waseleka ngemithwalo emihlane yethu.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Wayekela abantu bakhwela bazehlela emakhanda ethu; sedlula phakathi komlilo lamanzi, kodwa wasiletha endaweni yenala.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Ngizakuza ethempelini Lakho lomnikelo wokutshiswa ngigcwalise izifungo zami Kuwe.
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Izifungo ezathenjiswa yizindebe zami lomlomo wami lapho ngisekuhluphekeni.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Ngizakuhlabela izifuyo ezinonileyo, lomnikelo wenqama; ngizanikela ngenkunzi kanye lembuzi.
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Wozani lilalele, lina lonke elimesabayo uNkulunkulu; wothani ngilitshele lokho angenzele khona.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Ngakhala Kuye ngomlomo wami; indumiso yakhe yayisolimini lwami.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Aluba ngangigcine isono enhliziyweni yami, iNkosi ngabe kayizange ingilalele;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
kodwa ngeqiniso uNkulunkulu walalela walizwa ilizwi lami ngikhuleka.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Kadunyiswe uNkulunkulu ongawulahlanga umkhuleko wami futhi ongagodlanga uthando lwakhe kimi.