< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Psalmus In finem, Canticum Psalmi resurrectionis. Iubilate Deo omnis terra,
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
psalmum dicite nomini eius: date gloriam laudi eius.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Dicite Deo quam terribilia sunt opera tua Domine! in multitudine virtutis tuae mentientur tibi inimici tui.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Omnis terra adoret te, et psallat tibi: psalmum dicat nomini tuo.
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Venite, et videte opera Dei: terribilis in consiliis super filios hominum.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Qui convertit mare in aridam, in flumine pertransibunt pede: ibi laetabimur in ipso.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Qui dominatur in virtute sua in aeternum, oculi eius super gentes respiciunt: qui exasperant non exaltentur in semetipsis.
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Benedicite Gentes Deum nostrum: et auditam facite vocem laudis eius,
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Qui posuit animam meam ad vitam: et non dedit in commotionem pedes meos.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Quoniam probasti nos Deus: igne nos examinasti, sicut examinatur argentum.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Induxisti nos in laqueum, posuisti tribulationes in dorso nostro:
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
imposuisti homines super capita nostra. Transivimus per ignem et aquam: et eduxisti nos in refrigerium.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Introibo in domum tuam in holocaustis: reddam tibi vota mea,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
quae distinxerunt labia mea. Et locutum est os meum, in tribulatione mea.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Holocausta medullata offeram tibi cum incenso arietum: offeram tibi boves cum hircis.
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Venite, audite, et narrabo, omnes qui timetis Deum, quanta fecit animae meae.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Ad ipsum ore meo clamavi, et exultavi sub lingua mea.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Iniquitatem si aspexi in corde meo, non exaudiet Dominus.
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
Propterea exaudivit Deus, et attendit voci deprecationis meae.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Benedictus Deus, qui non amovit orationem meam, et misericordiam suam a me.

< Masalimo 66 >