< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
全地よ神にむかひて歓びよばはれ
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
その名の榮光をうたへその頌美をさかえしめよ
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
かみに告まつれ 汝のもろもろの功用はおそるべきかな大なる力によりてなんぢの仇はなんぢに畏れしたがひ
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
全地はなんぢを拝みてうたひ名をほめうたはんと (セラ)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
來りて神のみわざをみよ 人の子輩にむかひて作たまふことはおそるべきかな
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
神はうみをかへて乾ける地となしたまへり ひとびと歩行にて河をわたりき その處にてわれらは神をよろこべり
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
神はその大能をもてとこしへに統治め その目は諸國をみたまふ そむく者みづからを崇むべからず (セラ)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
もろもろの民よ われらの神をほめまつれ神をほめたたふる聲をきこえしめよ
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
神はわれらの霊魂をながらへしめ われらの足のうごかさるることをゆるしたまはず
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
神よなんぢはわれらを試みて白銀をねるごとくにわれらを錬たまひたればなり
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
汝われらを網にひきいれ われらの腰におもき荷をおき
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
人々をわれらの首のうへに騎こえしめたまひき われらは火のなか水のなかをすぎゆけり されど汝その中よりわれらをひきいたし豊盛なる處にいたらしめたまへり
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
われ燔祭をもてなんぢの家にゆかん 迫りくるしみたるときにわが口唇のいひいでわが口ののべし誓をなんぢに償はん
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
われ燔祭をもてなんぢの家にゆかん 迫りくるしみたるときにわが口唇のいひいでわが口ののべし誓をなんぢに償はん
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
われ肥たるものを燔祭とし牡羊を馨香として汝にささげ牡牛と牡山羊とをそなへまつらん (セラ)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
神をおそるる人よ みな來りてきけ われ神のわがたましひのために作たまへることをのべん
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
われわが口をもて神によばはり また舌をもてあがむ
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
然るにわが心にしれる不義あらば主はわれにききたまふまじ
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
されどまことに神はききたまへり聖意をわがいのりの聲にとめたまへり
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
神はほむべきかな わが祈をしりぞけず その憐憫をわれよりとりのぞきたまはざりき

< Masalimo 66 >