< Masalimo 66 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
[Tell] everyone on the earth that they should sing joyfully to praise God!
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
They should sing songs that say that God [MTY] is very great, and they should tell everyone that he is very glorious!
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
They should say to God, “The things that you do are awesome! You are very powerful, with the result that your enemies (cringe/bow down) in front of you.”
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Everyone on the earth [should] worship God and sing to praise him and honor him [MTY].
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Come and think about what God has done! Think about the awesome things that he has done.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
He caused the [Red] Sea to become dry land, [with the result that our] ancestors were able to walk right through it. There we rejoiced because of what he [had done].
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
By his great power he rules forever, and he keeps watching all the nations [to see what things they do], [so] those nations that want to rebel [against him] should not be proud.
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
You people [of all nations], praise our God! Praise him loudly in order that people will hear you as you praise him.
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
He has kept us alive, and he has not allowed us to (stumble/be defeated).
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
God, you have tested us; you have allowed us to experience great difficulties [to make our lives become pure] as [people] put precious metals in a hot fire [to burn out what is impure] [MET].
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
[It is as if] you allowed us to fall into traps [MET], and you [forced us to endure difficult things which were like] putting heavy loads on our backs [MET].
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
You allowed [our] enemies to trample on us; we [experienced difficulties/troubles that were like] [MET] walking through fires and floods, but now you have brought us into a place where we have plenty.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
[Yahweh], I will bring to your temple offerings that are to be completely burned [on the altar]; I will offer to you what I promised.
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
When I was experiencing [much] trouble, I said that I would bring offerings to you [if you rescued me]; [and you did rescue me, so] I will bring to you what I promised.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
I will bring sheep to be burned on the altar, and I will [also] sacrifice bulls and goats, and when they are burning, [you will be pleased when] the smoke [rises up] ([to you/to the sky]).
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
All you [people] who revere God, come and listen, and I will tell you what he has done for me.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
I called out to him to help me, and I praised him while I was speaking to him [MTY].
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
If I had ignored the sins that I had committed, the Lord would not have paid any attention to me.
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
But because [I confessed my sins], God has listened to me and he paid attention to my prayers.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
I praise God because he has not ignored my prayers or stopped faithfully loving me.