< Masalimo 66 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
to/for to conduct song melody to shout to/for God all [the] land: country/planet
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
to sing glory name his to set: put glory praise his
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
to say to/for God what? to fear: revere deed your in/on/with abundance strength your to deceive to/for you enemy your
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
all [the] land: country/planet to bow to/for you and to sing to/for you to sing name your (Selah)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
to go: come! and to see: see deed God to fear: revere wantonness upon son: child man
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
to overturn sea to/for dry land in/on/with river to pass in/on/with foot there to rejoice in/on/with him
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
to rule in/on/with might his forever: enduring eye his in/on/with nation to watch [the] to rebel not (to exalt *Q(K)*) to/for them (Selah)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
to bless people God our and to hear: hear voice: sound praise his
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
[the] to set: put soul our in/on/with life and not to give: allow to/for yoke foot our
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
for to test us God to refine us like/as to refine silver: money
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
to come (in): bring us in/on/with net to set: put distress in/on/with loin our
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
to ride human to/for head our to come (in): come in/on/with fire and in/on/with water and to come out: send us to/for abundance
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
to come (in): come house: home your in/on/with burnt offering to complete to/for you vow my
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
which to open lips my and to speak: promise lip my in/on/with distress to/for me
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
burnt offering fatling to ascend: offer up to/for you with incense ram to make cattle with goat (Selah)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
to go: come! to hear: hear and to recount all afraid God which to make: do to/for soul my
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
to(wards) him lip my to call: call out and extolling underneath: under tongue my
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
evil: wickedness if to see: select in/on/with heart my not to hear: hear Lord
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
surely to hear: hear God to listen in/on/with voice prayer my
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
to bless God which not to turn aside: turn aside prayer my and kindness his from with me