< Masalimo 66 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
“To the chief musician, a song or psalm.” Shout joyfully unto God, all ye lands:
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Sing forth the glory of his name; make glorious his praise.
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Say unto God, How fear-inspiring is every one of thy works! through the greatness of thy strength will thy enemies yield feigned obedience unto thee.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
All the lands shall bow themselves down unto thee, and shall sing praises unto thee; they shall sing praises to thy name. (Selah)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Come and see the deeds of God: fear-inspiring is his doing toward the children of men.
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
He changed the sea into dry land: through the river they went on foot: there did we rejoice in him.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
He ruleth by his might for ever; his eyes look upon the nations: the rebellious—these shall not be exalted. (Selah)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Bless, O ye people, our God, and cause the voice of his praise to be heard:
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
Who hath appointed our soul to life, and hath not suffered our foot to slip.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
For thou hast proved us, O God: thou hast refined us, as silver is refined.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Thou hast brought us into the net; thou hast placed fetters upon our loins.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Thou hast caused men to ride on our head: we entered into fire and into water; but thou broughtest us out to [the enjoyment] of overflowing plenty. a
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
I will enter thy house with burnt-offerings: I will pay unto thee my vows,
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Which my lips have uttered, and my mouth hath spoken, when I was in distress.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Burnt-offerings of fatlings will I offer up unto thee, with the incense of rams; I will prepare steers with he-goats. (Selah)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Come, hear, and I will relate, all ye that fear God, what he hath done for my soul.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Unto him I cried with my mouth, and a song of extolling was on my tongue.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
If I had looked on wickedness with my heart, the Lord would not have heard;
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
But verily God hath heard; he hath listened to the voice of my prayer.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Blessed be God, who hath not removed my prayer [from him], nor his kindness from me.