< Masalimo 66 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
Kuom jatend wer. Wer. Zaburi. Go koko gi mor ne Nyasaye, in piny duto!
2 Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
Wer kipako duongʼ mar nyinge; mi pakne obed gi duongʼ!
3 Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
Wachne Nyasaye niya, “Mano kaka timbe mitimo dongo! Tekoni duongʼ manade, mamiyo wasiki duto leny nono koneni.
4 Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
Piny duto kuloreni; giweroni wende pak; giwero wende pak ka gipako nyingi.” (Sela)
5 Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
Biuru uneye gik ma Nyasaye osetimo; bi uneye kaka gik motimo ne dhano dongo!
6 Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
Ne oloko nam lo motwo, mine gikalo pige ka giwuotho gi tiendegi, Biuru mondo wabed moil kuome.
7 Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
Olocho nyaka chiengʼ gi teko ne, wengene ema rito ogendini. Omiyo kik jongʼanyo hedhre mar kedo kode. (Sela)
8 Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
Pakuru Nyasachwa, yaye ogendini, neuru ni pak mipakego ji duto owinjo;
9 Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
oserito ngimawa kendo osegengʼo tiendewa ni kik kier.
10 Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
Yaye Nyasaye ne itemowa ni in iwuon; ne ipwodhowa ka fedha.
11 Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
Ne iterowa e od twech kendo ne iketo lodi mapek e dier ngʼewa.
12 Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
Ne imiyo ji onyono wiyewa; kendo ne wakalo mach gi pi, kata kamano ne ikelowa nyaka kama omew.
13 Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
Abiro biro e hekalu mari gi misango miwangʼo pep kendo abiro chopo kwongʼruok masetimo kodi.
14 Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
Kwongʼruok mane asingoni e chunya kendo awacho gi dhoga kane an e thagruok.
15 Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
Abiro timoni misango gi jamni machwe kendo abiro miyi chiwo mar imbe; bende abiro chiwoni rwedhi gi diek. (Sela)
16 Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
Biuru uchik itu, un duto muluoro Nyasaye; we anyisue gik ma osetimona.
17 Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
Ne aywakne gi dhoga; pakne ne ni e lewa.
18 Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
Ka dine bed ni amor gi richo manie chunya, to Ruoth dine ok ochikona ite,
19 koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
to kuom adier, Nyasaye osechikona ite kendo osewinjo dwonda ka alame.
20 Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!
Pak obed ne Nyasaye, ma ok osedagi lamona, kata golo herane kuoma.

< Masalimo 66 >